Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 98

Paphata pa Chichewa Kodyakokha: Mkazi wosakwatiwa, mbeta. Chitsanzo: (a) Tabwera kwanu kuno chifukwa tamva zoti kuli kodya kokha. (2) Makolo amada nkhawa, anyamata akamapanda kuzungulirazungulira pakhomo pamwe pali kodya kokha. Koka fodya: Kusuta fodya. Chitsanzo: Amisala ambiri omwe ali m’taunimu anayamba kukoka fodya wamkulu atauzidwa kuti amapatsa nzeru. Koka mtima: Kukusangalatsa n’kufika potengeka nayo. Chitsanzo: Nyimboyi yandikoka mtima. Koka mtsonyo: Kutsonya, kuchita mwano. Chitsanzo: Mayi ophika mowa aja amadziwa kuukoka mtsonyo. Koka utsi: Suta fodya. Chitsanzo: Munthu amene amakoka utsi sasowa. Kokera kwako: Kuchita kapena kunena chinthu kuti chikuyendere bwino kuposa anzako. Chitsanzo: Achuma ambiri ndi adyera, amangokokera kwawo. Kokomeza nkhani: Kuwonjezera zina ndi zina munkhani. Chitsanzo: Amanena kuti mmene anadera, ayenera kuti amamva kupweteka. Koma ine ndimaona kuti akokomeza nkhani. Kola chona: Kupalamula. Chitsanzo: Ukapitiriza zimenezi ukola chona. Kolola: (a) Kukutengera ndalama zonse. 97