Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 97

Paphata pa Chichewa Khwasula m’kamwa: Dyera nyama. Chitsanzo: Madzulo ano tikhwasula m’kamwa. Khwasula: Kutsinkha ndiwo. Chitsanzo: Anawa akungokhwasula ndiwo. Khwenya: Kudya mango akupsa popanda mpeni. Chitsanzo: M’nthawi ya njala timapulumukira kukhwenya. Khwima m’manja: Kuzolowera kugwira ntchito zovuta. Chitsanzo: Ntchito zake zikufuna anthu okhwima m’man- ja. Khwimbi la anthu (namtindi wa anthu, fumbi, khamu la mnzanga ali pati, khamu la mundipondera mwana): Anthu osawerengeka, anthu ambiri. Chitsanzo: Kumaliroko kunali khwimbi la anthu/namtindi wa anthu/fumbi/khamu la mnzanga ali pati/khamu la mundipondera mwana. Khwinthi: Kususuka. Chitsanzo: Mwanayu ndi wakhwinthi. Kiyama: Zoopsa. Mawu amenewa anayamba chifukwa cha mawu omwe achisilamu amagwiritsa ntchito ponena za mapeto a dzikoli. Chitsanzo: Mukamanditengera maso m’mwamba, ndikuonetsani kiyama. Kodi mumaweta akalulu? Mawu amene amanenedwa moseka, ponyoza munthu amene wagula masamba ambiri oti akaphike kunyumba kwake. Chitsanzo: Ndimadabwa kuti kodi mumaweta akalulu? Masamba onsewa ndi a chiyani? 96