Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 94
Paphata pa Chichewa
(2) Anthu ankadana aja pano ali khethekhethe.
(b) Kuyang’ana mophethiraphethira.
Chitsanzo: Atamuwaza mbamalo amangoti khethekhethe.
Khofi:
(a) Chibakera.
Chitsanzo: Anamupatsa khofi.
(b) Mtundu wa chakumwa chokhala ngati tiyi chomwe
chimakhala chakuda komanso chowawa.
Chitsanzo: Ndikufuna kumwa khofi.
Kholophethe: Kubereka kwambiri, zambiri.
Chitsanzo: (1) Mango angoti kholophethe m’mitengo. (2) Zi-
patso pakhomo pawo zangoti kholophethe.
Khoma malata m’mutu: Kukhala ndi dazi.
Chitsanzo: Ana ambiri a masiku ano sakumachedwa ku-
khoma malata m’mutu.
Khoma ndawala: Kuyenda mofulumira kwambiri.
Chitsanzo: Ndakumana nawo ataikhoma ndawala.
Khomera kudowa: Kukhala wosabereka.
Chitsanzo: Akuti asiyana ndi amuna awo chifukwa ana-
khomera kudowa.
Khonyola:
(a) Kuvulaza.
Chitsanzo: Akadzakuuza kuti unyamule mwanayu
udzamugwire bwino kuopera kuti ukhoza kudzamu-
khonyola.
(b) Kuthyola
Chitsanzo: Ndamuona akukhonyola chimanga.
93