Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 93
Paphata pa Chichewa
Khalira khuthe: Kukhala pamavuto.
Chitsanzo: Anthuwa akukhalira khuthe.
Khalira m’phanthi: Khala mozunzika.
Chitsanzo: Ukakhala mkamwini, umangokhalira
m’phanthi.
Khalukhalu: Utangokhala pang’ono.
Chitsanzo: Khalukhalu, tinangoona atulukira!
Khambi: Kusafuna kumvera, ena amati liuma.
Chitsanzo: M’tauni muno simufuna munthu wakhambi,
akhoza kulisiya dzikoli ndithu.
Khamitsa mate (malovu): Kufunsa mafunso mosalekeza.
Chitsanzo: Pakhomo pano pakabwera a Mboni ndi-
wakhamitsa malovu.
Khapa mtengo: Tchaja mtengo wokwera kwambiri.
Chitsanzo: Mukapanda kuchenjera akukhapani chimtengo
chodula.
Khatcha mbama: Menya mbama. Mawu achipongwe ko-
manso okokomeza onena za munthu akamenya mnzake
mbama.
Chitsanzo: Ndinawaona aphunzitsi akumukhatcha
mbama.
Khaulitsa: Lapitsa, kumvetsa wina kupweteka.
Chitsanzo: Wakubayo anamukhaulitsa pomusenzetsa
katundu yemwe anabayo.
Khethekhethe:
(a) Kugwirizana kwambiri.
Chitsanzo: (1) Panopa aboma komanso azipembedzo ali
khethekhethe.
92