Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 90
Paphata pa Chichewa
Kapitawo: Munthu wosabereka.
Chitsanzo: Amene ajatu ndi akapitawo, ntchito yawo ndi
kulondolera akazi awo aja basi.
Kapolo: Munthu wovutika, wosauka, munthu yemwe
amagwira ntchito koma osapeza kanthu.
Chitsanzo: Unganene chiyani kapolo ngati iwe!
Kapondam’zichiri: Munthu woyendayenda.
Chitsanzo: Usadzayerekeze kukwatiwa ndi
kapondam’zichitiri. Udzangokhala mulonda wa nyumba
yake.
Kapsala: Munthu wakuba.
Chitsanzo: (a) Pakampani pano sitikufuna kumasunga
akapsala. (b) Kuti akapsala asakubere, umafunika kuika
ndalama m’kabudula wamkati kapena mukhamisolo.
Kapunthabuye: Munthu wosauka.
Chitsanzo: Ndingawapatse chiyani kapunthabuye ngati
ine!
Kasiyagoli: Munthu amene amaba koma m’kuthawa
mosadziwika bwino.
Chitsanzo: Apolisi anakhwimitsa chitetezo atazindikira
kuti munthu wina ndi kasiyagoli.
Katakwe: Katswiri.
Chitsanzo: (1) Amene uja ndi katakwe pa nkhani yokonza
njinga. (2) Akazi anu aja ndi katakwe popeka bodza.
Katangale: Kupereka ndalama kuti akuchitire zinazake.
Chitsanzo: (1) Boma lalonjeza kuti lithana ndi anthu onse
a katangale. (2) Kulemera kujatu ndi katangale!
89