Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 87
Paphata pa Chichewa
Kana kali kutsaya: Kukana zimene uzidziwa kapena
wachita.
Chitsanzo: Ndalama zanu watenga ndi yemweyu, kungoti
akukana kali kutsaya. Musecheni mumugwira nayo.
Kana m’maso muli gwa: Kukana ukudziwapo kanthu,
kukanitsitsa mopanda manyazi.
Chitsanzo: Satana ananena kuti Yobu adzamukana
Mulungu m’maso muli gwa.
Kana moto: Kukanika kupsa.
Chitsanzo: (1) Chikunichi chakana moto. (2) Nsimayi
yakana moto.
Kana poyera: Kukana pagulu.
Chitsanzo: Mkazi wako akakukana poyera, umafunika
kungomusiya kuti adziwe mmene umbeta umawawira.
Kanda padazi: Kuputa munthu.
Chitsanzo: (a) Angabwere pakhomo panga pano
n’kumandikanda padazi? (2) Si bwino kumawakanda
anzako padazi.
Kandionamaso: Kuchita kanthu chifukwa cha kuonana.
Chitsanzo: Ndikadapanda kukuitanani mukanandipatsa
moni inu? Moni wanuyutu ndi wa kandionamaso.
Kangalika: Kulimbikira.
Chitsanzo: Mukakhala okangalika akukwezani pantchito.
Kangandiwamba: Munthu womana kwambiri,
waumbombo.
Chitsanzo: (1) Amene uja ndi kangandiwamba, dzulo
zathu timadyera limodzi, lero zake akudyera kuchipinda.
86