Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 85

Paphata pa Chichewa Kalulu khonje (kaponda nazale): Mphaka. Mawu onena mwachining’a omwe ena amagwiritsa ntchito ponena za mphaka amene akufuna kumupanga ndiwo. Mawuwa amakonda kugwiritsidwa ntchito ndi angoni. Chitsanzo: Kodi unamulawapo kalulu khonje? Kama: (a) Bedi. Chitsanzo: Ndidzakwatira ndikadzagula kama. (b) Kukama chiweto kuti chitulutse mkaka. Chitsanzo: Ndisadzayerekeze kukupeza ukukama mkaka. (c) Kutengera munthu zinthu zambiri. Chitsanzo: Akungofuna kundikama ndalama zanga. Kamatewe: Munthu wamatewe. Chitsanzo: Kamatewe uja wabweranso. Kamathigidi: Munthu wamatekenya. Chitsanzo: Kamathigidiyo asalowe m’nyumba muno. Kamatule: Munthu wakuba. Chitsanzo: Akamatule ambiri masiku ano akumabwera atavala masuti. Ukamazindikira kuti akubera mumakhala m’mbuyo mwa alendo. Kamba anga mwala: Nkhani zina ndi zovuta kuzimvetsa. Chitsanzo: Zina ukanenena abale! Kamba anga mwala ndithu. Kamba: (a) Chakudya cha paulendo. Chitsanzo: Ndanyamulako kamba kuti njala ikandiwawa ndidye. (b) Fulu. Chitsanzo: Ndinakumana naye atanyamula kamba. 84