Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 81
Paphata pa Chichewa
Kabanga: Mowa.
Chitsanzo: Amakonda kumwa kabanga.
Kabwerebwere: Munthu womangopitapita kwinakwake.
Chitsanzo: (1) Uyu ndi kabwerebwere kundende kuno. (2)
Sitifuna akabwerebwere pamudzi pano.
Kabweremawa: Chinthu chosalimba.
Chitsanzo: Usadzagule nsalu m’mashopu amene aja,
zinthu zimene amagulitsa ndi za kabweremawa.
Kacherezera kankhani: Kunena nkhani moti wina
imuipire.
Chitsanzo: Amafuna kuti ziwakomere, n’chifukwa chake
anayamba kucherezera kankhani.
Kadam’manja: Munthu wosauka kwambiri.
Chitsanzo: Sindingakwatiwe ndi kadam’manja.
Kadangoyenda: Mawu amenewa amanenedwa zikakhala
kuti mkazi wokwatiwa sakutenga pakati.
Chitsanzo: Ndimaganiza kuti pofika pano akhala ataima,
koma ayi ndithu, kadangoyenda.
Kadaulo: Munthu waluso kwambiri pantchito yake.
Chitsanzo: Ameneyu ndi kadaulo wosema ziboliboli.
Kadaundamadzi: Nsima.
Chitsanzo: Ndigule nkhuni pansikapa kuti ndikaphike
kandaundamadzi.
Kaduka kachinangwa: Nsanje yaikulu.
Chitsanzo: Sindingakhale pamudzi pa anthu a kaduka
kachinangwa.
80