Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 77
Paphata pa Chichewa
Imandimaliza: Imandisangalatsa.
Chitsanzo: (1) Ndemanga imene anapereka inandimaliza
kwabasi. (2) Mwana amene uja amandimaliza.
Imba mwiyo: Kunena zinthu monyozera ndiponso
mosatsimikiza.
Chitsanzo: Akayamba kuimba mwiyo amakhala kuti
akulipeka bodza.
Imba ng’oma yowambawamba: Chita zinthu zimene
mnzakoyonso amafuna.
Chitsanzo: Atamufunsira anayankha mwamunayo kuti,
“Mwaimba ng’oma yowambawamba.”
Ipha mpola: Kupumula, kupitidwa mphepo ina.
Chitsanzo: (1) Ndipite kunyanja kuti ndikaphe mpola. (2)
Sindikufuna kumagwira ntchito yokhetsa thukuta ena
akungopha mpola.
Ipha tsogolo: Kuwononga mwayi womwe
ukanakuthandiza m’tsogolo, kuwononga tsogolo.
Chitsanzo: Aphunzitsi amene amagona ndi ana a sukulu,
amakhala akuwaphera tsogolo lawo.
Ipitsa:
(a) Pereka mimba.
Chitsanzo: Zikumveka kuti mwana wanuyu ndi amene
waipitsa mtsikana uja.
(b) Kuononga mbiri ya munthu wina.
Chitsanzo: Ulendo anapita kumudzi uja anakatiipitsako.
Ipsa n’kumbuyo komwe: Kuvutika kwambiri.
Chitsanzo: Anzanu aja anapsa n’kumbuyo komwe akuba
atawabera katundu yense.
76