Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 76

Paphata pa Chichewa Chitsanzo: Mwana wanu mukumuikira kumbuyoyu adzakugalukirani tsiku lina. Ili m’mazira: Mawuwa amakonda kunenedwa zikakhala kut nkhani inayake ikanaganiziridwabe kapena ikakhala kuti sinatuluke. Chitsanzo: Akuboma akungoti nkhaniyi idakali m’mazira. Kaya adzaticheukira liti. Ili mkati: Mawuwa amanenedwa ndi munthu amene akugwira ntchito kapena amene akuona anzake akugwira ntchito. Anganenedwe pouza munthu kuti ali pakati pogwira ntchitoyo kapena anawapeza akugwira ntchito. Chitsanzo: Ndimaganiza kuti ndikawapeza asanayambe, koma ndinapeza ili mkati. Ima mutu: Kusowa chochita. Chitsanzo: Ndilibe ndalama zolipirira njinga ndaonongayi, moti mutu wanga waima. Kaya ndikaziba kuti ndalama ine? Ima nazo: Akaiyamba ndewu sagwirika, sathawa. Chitsanzo: Ngakhale anamumenya ndi kuseri kwa chikwanje, sanaimve moti nayenso anayamba kudzipulumutsa zibakera. Mwana amene uja amaima nazo zibakera. Ima pachulu: Kulalatira. Chitsanzo: Musayerekeze kuwaputa, akuimirani pachulu. Ima: Tenga pakati. Chitsanzo: Mayi akaima amafuna zakudya zachilendo monga ziboda za nkhumba, dothi komanso amafuna kumva fungo la dizilo. 75