Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 75
Paphata pa Chichewa
Igwa apa: Mawuwa amakonda kunenedwa pamlandu
pouza munthu kuti alipire chifukwa cha mlandu umene
wapalamula.
Chitsanzo: Zaonekeratu kuti unaba nzimbe ya eni ndi iwe.
Igwa apa! nkhuku ziwiri.
Igwa chagada: Lephera kotheratu.
Chitanzo: Amayesa kuchita zinthu zosatheka, lero agwa
chagada.
Igwa nkhope: Kuchita manyazi.
Chitsanzo: Atamutulukira kuti amanama, mnyamatayo
anagwetsa nkhope.
Ika pachidale: Pangitsa kuti munthu asowe pothawira.
Chitsanzo: Lero sanauone mpira chifukwa otseka
kumbuyo anamuika pachidale.
Ika pakona: Kupanikiza munthu, kupangitsa kuti zinthu
zisayendere bwino wina.
Chitsanzo: (1) Zimene anena zija zatiika pakona. (2) Koma
ndiye mwatiika pakonatu anzanufe.
Ikakuona litsiro sikata: Mavuto akati akupanikize
satherapo.
Chitsanzo: Anthuni ndikukumana ndi mavuto ine!
Zikungokhala ngati ndalumpha m’chiwaya n’kugwera
pamoto. Ndithudi, ikakuona litsiro sikata.
Ikidwa pampani: Kupanikizidwa moti sungathawe.
Chitsanzo: Anasiya kuyendayenda masiku ano, akazi awo
anawaika pampani.
Ikira kumbuyo (ika kumbuyo): Kuteteza munthu,
kumutchinjiriza.
74