Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 70
Paphata pa Chichewa
(b) Munthu amene amanyengerera akazi n’cholinga choti
achite nawo zopusa.
Chitsanzo: Pamudzi pano sitisekerera a gwamula.
Gwanda (shati): Kudula munthu manja kapena mikono.
Chitsanzo: (1) Wakuba uja amupatsa gwanda. (2)
Ukapitiriza moyo wakubawu anthu adzakugulira shati.
Gwedeza mbina: Yenda moyerekedwa. Mawuwa
amanenedwa makamaka kwa akazi.
Chitsanzo: Mukumupatsa matama ndi inuyo, n’chifukwa
chake akugwedeza mbina.
Gwedeza mutu: Vomera.
Chitsanzo: Ndimadana ndi munthu woti azingogwedezera
mutu pa chilichonse.
Gwera pamphuno: Kukumana ndi mavuto n’kusowa
nawo chochita, kukumana ndi mavuto mwadzidzidzi.
Chitsanzo: Mavutowa atigwera pamphuno.
Gwerula nkhwanga n’chambuyo (chumba): Kukhala
wosabereka.
Chitsanzo: Bambo amene aja anagwerula (gulula)
nkhwanga n’chambuyo.
Gwerulana mano: Chotsana mano.
Chitsanzo: Akawasiya osawaleletsa agwerulana mano.
Gwetserana mumchenga: Kukambirana nkhani inayake,
kuthetsa mkangano.
Chitsanzo: Akufuna kuti tigwetserane mumchenga.
Gwidiza: Meza.
Chitsanzo: Ndamupeza akugwidiza thobwa lija.
69