Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 56
Paphata pa Chichewa
nkhaniyi yandidzera kunkhongo?
Dziko lidakali mphonje: Kalekale zinthu zisanasinthe
mmene zilili masiku ano. Dziko lidakali losiyana ndi
limene lili pano.
Chitsanzo: Padangotero! Kalekalelo dziko lidakali mphonje,
kunali kalulu ndi fisi.
Dziko lidzatha: N’kosatheka kapena n’zokayikitsa.
Mawuwa anganenedwe ponena kuti zinazake zitachitika,
dziko likhoza kutha.
Chitsanzo: Sangabwere kuno amene uja. Akadzabwera
dziko lidzatha.
Dziko likali nsoka: Kalekale zinthu zisanasinthe mmene
zilili masiku ano.
Chitsanzo: Zimenezi zinachitika dziko likali nsoka.
Dziko: Anthu.
Chitsanzo: Atakana kukachita maphunziro apamwamba
kunja, dziko linadabwa naye kwambiri.
Dziko: Manda. Mawu amenewa amagwiritsidwa ntchito
kuti ana asadziwe kumene mumakaika munthu akafa.
M’buyomu ana ankatsekeredwa m’nyumba pakhomo
pakachitika maliro ndipo sankaloledwa kupita kumanda
chifukwa cha zikhulupiriro zina.
Chitsanzo: Mpofunika tipite kudziko kuti ndikakuonetseni
pomwe m’bale wanu anagona.
Dzimverem’tolo: Mawuwa amanenedwa pofuna
kutsindika mfundo yakuti munthuyo wadzimvera yekha.
Chitsanzo: Apatu ndiye dzimveremtolo, musiye khalidwe
loipali.
55