Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 51
Paphata pa Chichewa
(2) Ameneyu ndi dolo wa galimoto.
(b) Munthu wautambwali yemwe amafuna kupusitsa ena.
Chitsanzo: M’taunimu mwachuluka madolo.
Dongolera: Kuchita zinthu zofunika, kuchita chinachake
mwanjira yabwino kwambiri.
Chitsanzo: Apa ndiye mwaidongoleratu, mpaka
kuphikiratu nsima!
Dontha: Kupusa.
Chitsanzo: Mtsikana amene uja ndi wodontha.
Dothi lokhalokha: Ambiri.
Chitsanzo: Kumsonkhanoko kunali dothi lokhalokha.
Dothi: Zochuluka.
Chitsanzo: Kumaliroko galimoto zinali dothi.
Dovu: Amatanthauza nkhuli.
Chitsanzo: Munthu wadovu sasangalala mukamuphikira
chitambe.
Duduluka: Kutengeka ndi zinthu.
Chitsanzo: Pakampani pano sitifuna anthu oduduluka.
Duka mikono: Kusowa chochita.
Chitsanzo: Vutoli latidula mikono.
Duka nzengo: Wamakhalidwe amphulupulu.
Chitsanzo: Mwana amene uja anaduka nzengo, sati
wapalamula liti.
Dula apa: Munthu woyendayenda.
Chitsanzo: Munthu akakhala dula apa sachedwa
kukumana ndi mavuto.
Dula mwana (tsempha): Kuchita chiwerewere mwana
wako ali m’chilowero kapena m’chikuta. Malinga
50