Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 50
Paphata pa Chichewa
kuwajeda, koma anadzidzimuka ataona mwini wakeyo
diso lili biriwiri. (2) Pamene ankamutengera nkhuku zake,
diso lake linali liri biriwiri.
Diso lili pamtunda:
(a) Munthu yemwe akuoneka mwankhawa.
Chitsanzo: Pamene amabwera n’kuti diso lili pamtunda.
(b) Akufuna kufa.
Chitsanzo: Tinawapeza atagwa pansi, diso lili pamtunda.
Mbatata ndi imene inawathimba pakhosi.
Diso lili piriwiri: Atatulutsa diso, maso atafiira.
Chitsanzo: (1) Mmene amafika kunyumba n’kuti diso lili
piriwiri. (2) Maso ake ali piriwiri ngati wasuta chamba.
Diso limodzi: Kuona pang’ono.
Chitsanzo: Alendo ajatu ndinangowaona diso limodzi.
Doda chikopa: Kumenya bwino mpira.
Chitsanzo: Anyamata a timu imeneyi amadoda chikopa.
Dodoma:
(a) Kuchita chibwibwi.
Chitsanzo: Amawerenga mododoma chifukwa cha mantha.
(b) Kudabwa.
Chitsanzo: Ndinadodoma nditawaona ali mimba
pamtunda.
Dokodoko (nokonoko): Kuda, uve, litsiro.
Chitsanzo: (1) Zovala zawo zinali zadokodoko. (2) Pakhomo
pawo ali ana a nokonoko.
Dolo:
(a) Katswiri.
Chitsanzo: (1) Amene uja ndi dolo pa nkhani ya mpira.
49