Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 47
Paphata pa Chichewa
Chokolo: M’zikhalidwe zina mwamuna akamwalira,
m’bale wake amakwatira mkaziyo ngakhale ali kale ndi
mkazi wina. Akatero timati mkaziyo walowa chokolo.
Chitsanzo: Mkaziyu analowa chokolo mwamuna wake
atatisiya.
Chopangitsa malovu thethethe m’kamwa: Chakudya
chokoma kwambiri.
Chitsanzo: Azakhali anatiphikira chakudya chopangitsa
malovu thethethe m’kamwa.
Chophwamphwanthika: Chophwanyika, chafulati.
Chitsanzo: Chigumu mwaphikachi ndi chophwam-
phwanthika.
Chophwathalala: Chopwanyika, chafulati, chodirizika.
Chitsanzo: Wanyamula chitsulo chophwathalala.
Chosakhala bwino:
(a) Choipa.
Chitsanzo: Khalidwe limene mwayambali ndi losakhala
bwino.
(b) Chakudya chosakoma kapena chowonongeka.
Chitsanzo: Chakudyachi ndi chosakhala bwino.
Chothyokathyoka: Chosamveka, chosalongosoka.
Chitsanzo: Amayankhula Chichewa chothyokathyoka.
Chotsa chimbenene: Kuchenjeretsa, kukhaulitsa,
kumenyedwa, kugonjetsedwa koopsa.
Chitsanzo: (a) Mnyamata woyerekedwa uja amuchotsa
chimbenene. (b) Abwere kuno timuchotse chimbenene.
Chotsa dalazi: Idya zankhuli.
Chitsanzo: Tikagule mutu wa mbuzi kuti tichotseko dalazi.
46