Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 407

Paphata pa Chichewa zimakhala zozizira. Zoziziritsa kukhosi (kum’mero): Chakumwa chokhazikitsa mtima pansi, zakumwa zopha ludzu. Chitsanzo: Ukatopa ndi dzuwa umafunika kudzipepesa pogula zakumwa zoziziritsa kukhosi. Zoziziritsa thupi: Nkhani zofooketsa, zochititsa mantha kapena manyazi. Chitsanzo: Zimene mwana ameneyu wachita ndi zoziziritsa thupi. Zozwetetsa mutu: Zosokoneza maganizo. Chitsanzo: Mavuto ndikukumana nawo ine ndi ozwetetsa mutu. Zukuta: Kuyang’anitsitsa chinthu kuti upezepo chifukwa, kukambirana mozama. Chitsanzo: Tiyeni tizukute nkhaniyi bwinobwino. Zula mano: Khaulitsa koopsa. Chitsanzo: Mukawatengera maso m’mwamba adzakuzulani mano. Zula mnzako minga yapamsana: Kuthandiza munthu. Minga yapansana imakhala yovuta kuzula chifukwa mkono sungafikepo. Choncho kuzula munthu wina minga ya pamsana ndi kumuthandiza kwambiri. Chitsanzo: Amene aja ndi amene anandizula minga yapansana. Zungulira ngati nguli: Kuzungulirazungulira. Chitsanzo: Osewera ena akamafuna kudyetsa njomva amazungulira ngati nguli. Zunguza lirime: Kugwiritsa ntchito lilime mochenjera. Chitsanzo: Pulezidenti uyu yekha ndiye amadziwa kuzunguza lirime. Zunguza mutu: Kusokoneza mutu. Chitsanzo: Samuyi ndi yozunguza mutu. 406