Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 399
Paphata pa Chichewa
Zibolobosha: Kulemba zinthu zosaoneka bwino.
Chitsanzo: Amangolemba zibolobosha.
Zidze pano n’zatonse: Mavuto akagwa timafunika
kuthandizana.
Chitsanzo: Adwala kwambiri moti m’pofunika kulimba
mtima. Zidze pano n’zatonse!
Zifuyo: Ziweto. Nthawi zina mawuwa amagwiritsidwa
ntchito ponena za agalu oweta. Akakhala ambiri ena
amangowanena kuti zifuyo.
Chitsanzo: Pakhomo pawo pali zifuyo.
Zigogodo: Zibakera, nthawi zambiri mawuwa amanena za
munthu wokonda ndewu.
Chitsanzo: Amuthamitsa anzake odziwa zigogodo.
Zijazi: Mawu omwe ena amanena ngati sakufuna
kutchula zinthu zinazake kapena ngati zinthuzo zili
zachinsinsi.
Chisanzo: Ubwere pa nthawi ya nkhomaliro, koma
usaiwale zijazi.
Zikhulupiriro zachikuda: Mawu amenewa amanena za
kukhulupirira za ufiti, matsenga komanso mizimu. Anthu
ambiri a ku Africa kuno amakhulupirira zimenezi
chifukwa ndi zimene makolo awo akhala
akuzikhulupirira.
Chitsanzo: Pamene amishonale ankabwera, anapeza
anthu akuda ali ndi miyambo yawo ndipo anayamba
kunena kuti zikhulupiriro zachikuda n’zosemphana ndi
mawu a Mulungu.
Zikusuntha? Zili bwino, zikuyenda bwino.
Chitsanzo: Ife zikungoyenda ngati nkhono, inu bwanji,
zikusuntha?
Zikuwayendera: Sakukumana ndi mavuto.
Chitsanzo: Kungoona mmene akuonekera
ukumadziwiratu kuti zikuwayendera.
398