Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 398

Paphata pa Chichewa Zayakunkhongo: Munthu wosamva za anzake, wosamvera. Chitsanzo: (1) Kodi zayakunkhongo uja ali kuti? (2) Ngakhale mumulangize saamva. Iye uja ndi zayakunkhongo. Zayakunkhongo: Munthu wosamva. Chitsanzo: Mwana ameneyu ndi zayakunkhongo, ngakhale mumuuze saamva. Zayang’ana kungolo: Zavuta. Mawuwa amayerekezera zimene zimachitika ng’ombe zikayang’ana kungolo. Chitsanzo: Atangotulukira ndinadziwa kuti zayang’ana kungolo. Zazii: Zopanda nzeru. Chitsanzo: Anabwera kunoko n’kumandiuza zazii. Zazira: Kalipira. Chitsanzo: Mukamasokosera akuzazirani. Zedi: Kuvomereza kuti ndi zoona, ndithu. Chitsanzo: Zedi, akunenadi zoona. Zembeneku: Kuthawa mofulumira. Chitsanzo: Anangoti zembeneku! Zemberana: Chita zachimasomaso, chita uhule. Chitsanzo: Bambo a pamtunda aja amazemberana ndi mlamu wawo. Zembetsa: Thawitsa mobisa, kulowetsa katundu mwachinyengo. Chitsanzo: (1) Ndani wazembetsa katunduyu? (2) Anthu ena akumazembetsa katundu waboma. Zembetsana: Kutengana mopanda dongosolo n’kumakhala ngati banja. Chitsanzo: Anazemetsana ndi mwamuna wamwini. Zibalobalo: Zipatso za mtengo. Nthawi zambiri sizidyedwa. Chitsanzo: Apulula zibalobalo zonse. 397