Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 396
Paphata pa Chichewa
Zakuvuta: Walephera.
Chitsanzo: Ngati umaganiza kuti undipusitsa, zakuvuta!
Zam’kutu: Zopanda nzeru, zosathandiza.
Chitsanzo: Nditakumana naye anayamba kundiuza
zam’kutu.
Zam’maluwa: Zabodza, zopanda pake.
Chitsanzo: Akukuuzanizi ndi zam’maluwa.
Zam’manja: Ndalama.
Chitsanzo: Anamulonjeza kuti amupatsa zam’manja.
Zam’mutu: Kuyankhula zopanda nzeru.
Chitsanzo: Zimene akuyankhula ndi zam’mutu.
Zamadulira: Zachidule.
Chitsanzo: Amayenda zamadulira, wakumana nazo.
Zambwerera: Zopusa.
Chitsanzo: Munthu wanzeru sayankhula zambwerera.
Zamoyo palibe: Zokayikitsa ngati atachire.
Chitsanzo: Apatu zamoyo ndiye palibe.
Zamtopola: Zachipongwe.
Chitsanzo: Anyamatawa akupitirizabe kuchita zamtopola.
Zamugwera: Wakumana ndi vuto.
Chitsanzo: Mnzanu uja zamugwera.
Zamwaanthu: Mavuto otumizidwa ndi anthu mosadziwika
bwino. Mawu amenewa amanenedwa chifukwa cha
zikhulupiriro zoti anthu ena amatha kulodza anzawo.
Chitsanzo: Ndi zamwaanthu izi, si mwati kuchipatala
sanakupezeni ndi matenda?
Zandisuntha: Zandikhudza, zandigwira mtima.
Chitsanzo: Nkhani ya mnyamatayo yandisuntha.
Zandithyola nkhongono: Zandifooketsa kwambiri.
Chitsanzo: Nkhaniyi yandithyola nkhongono.
395