Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 394
Paphata pa Chichewa
Yokoka ngolo: Mawu amenewa amatanthauza kuti ndi
nyama yolimba. Nthawi zambiri nyama imene imakoka
ngolo imakhala yolimba mnofu kwambiri.
Chitsanzo: Nyamayi inali yokoka ngolo.
Yophera awemba: Bodza lomwe munthu amanena
kapena zinthu zina zomwe munthu amachita pofuna
kupusitsa mnzake. Mawuwa angananenso zinthu zimene
wina angachite ngati pongobisalira zolinga zake zili zina.
Chitsanzo: Mumaganiza kuti ndikudwaladi, inali yophera
awemba!
Yosagwira: Zoti sizingathandize, si zomveka.
Chitsanzo: Imeneyo ndi yosagwira, sindingatsuke mbale
komanso kukolopa m’nyumba iweyo uli khale!
Yosipa (wosipa): Kudya nsoma yopanda ndiwo.
Chitsanzo: Akudya nsima yosipa.
Yotentha: Yopezetsa ndalama.
Chitsanzo: Ayamba bizinezi yotentha.
Yudasi: Munthu amene amam’pereka mnzake ngati
mmene anachitira mwini dzinali.
Chitsanzo: Munthu ameneyu ndi Yudasi ndithu,
osamumvera chisoni mnzake?
393