Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 392
Paphata pa Chichewa
Yedzeka: Kutula pansi, kuyedzamiritsa kamtengo.
Chitsanzo: Yedzekani katunduyo apa.
Yenda chining’a: Kuchita chinyengo.
Chitsanzo: Kodi nanunso mwayamba kuyenda chining’a.
Yenda chogona: Mwalira.
Chitsanzo: Mudzandilira ndikadzayenda chogona.
Yenda m’mapazi: Kuzonda munthu, kukulondalonda.
Chitsanzo: Sindingamacheze nawo chifukwa amandiyenda
m’mapazi.
Yenda mahala: Kusapeza chomwe umayendera.
Chitsanzo: Ndinapita kumudzi kuti ndikagule chimanga,
koma ndayenda mahala.
Yenda moyera: Kusavutika kwenikweni ukamachita
zinthu.
Chitsanzo: Mukuyenda moyera chifukwa ine ndinakhetsa
thukuta.
Yenda ndi msana: Kunyada kosasamala nako za ena.
Chitsanzo: Kodi munthu ukalemera ndiye uyambe
kuyenda ndi msana?
Yenda pamtsetse: Mawuwa amanenedwa zinthu
zikamayendera munthu wina.
Chitsanzo: Masiku ano akuyenda pamtsetse.
Yenda paphazi: Kudana ndi munthu.
Chitsanzo: (1) Anyamata aja ayamba kuyendana paphazi.
(2) Anthu amene ndimakhala nawo moyandikana nyumba
andiyenda paphazi.
Yenda utsi uli tsitu: Kuyenda mopusa.
Chitsanzo: Ichi ndiye ndi chitsiru, chimangoyenda utsi uli
tsitu.
Yenda zochizochi: Yenda mwamanyazi.
Chitsanzo: N’chifukwa chiyani masiku ano akumayenda
zochizochi?
391