Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 391
Paphata pa Chichewa
Yang’ana nkhope: Kuchitira kanthu poyang’ana kuti uyu
ndi ndani.
Chitsanzo: Amfumu akamagawa makuponi
akumayang’ana nkhope.
Yang’anitsa kutali: Chenjeretsa.
Chitsanzo: Anzawo anawayang’anitsa kutali.
Yanika inswa: Kukhala bwino, kukhala momasuka.
Chitsanzo: Chigawengacho chitamangidwa, anthu
anayamba kuyanika inswa.
Yankho lothetsa makani: Yankho loti winayo
sanganeneponso kanthu.
Chitsanso: Anamupatsa yankho lothetsa makani.
Yankhulitsa pambali: Kuchititsa kuti wina ayankhule
mosakhala bwino, kupsetsa mtima.
Chitsanzo: Akufuna andiyankhulitse pambali kuti akapita
kumudziko azikanena kuti ndine woipa.
Yanokola: Yafa, yasiya kugwira ntchito.
Chitsanzo: Galimoto yanga yanokola.
Yatsa moto: Danitsa, yambanitsa.
Chitsanzo: Pamudzi panu paja pali munthu wina yemwe
akuyatsa moto.
Yauma: Yatha, yavuta.
Chitsanzo: Akangopanda kubwera ndiye kuti ntchito yake
yauma.
Yavi: Kungoti mbwee, balalabalala, kukhala
mosalongosoka.
Chitsanzo: (1) Tsitsi lawo langoti yavi! (2) Tathumulani
ulusi wangoti yaviwu.
Yedzeka ana: Bala ana okongola
Chitsanzo: Banja limene lija linayedzeka anyamata
okhaokha.
390