Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 387

Paphata pa Chichewa Wosokonekera: Wopanda khalidwe. Chitsanzo: Ali ndi mwana m’modzi yekha koma ndi wosokonekera. Wosunga malamulo: Womvera malamulo. Chitsanzo: Pasukulu pano tikufuna ana osunga malamulo. Wosunga pakamwa: Wosakonda kuyankhula nkhani zachinsinsi. Chitsanzo: Mwana ameneyu ndimamukhulupirira, ndi wosunga pakamwa. Wosweka mutu: Wolongolola, wovuta. Chitsanzo: Atsikana ambiri amakhala osweka mitu. Wotakata: Wachimasomaso. Chitsanzo: Ndamva kuti ukuyenda ndi mtsikana wotakata uja, samala utenga zosatenga. Wothetsana: Kukangana kwambiri. Chitsanzo: Ankhonswe anatopa nawo, amangokhalira kuothetsana nthawi zonse. Wothirathira thendo kale: Mtsikana wamkulu, mtsikana wotha msinkhu, mbeta. Chitsanzo: Kunyumbaku kuli wothirathira thendo kale. Wotisonkhera moto: Mtsikana wosakwatiwa kapena kuti mbeta. Chitsanzo: Tabwera kwanu kuno kuti tidzapeze wotisonkhera moto. Wotopa ndi mphasa: Munthu yemwe wadwala kwa nthawi yaitali. Chitsanzo: Ndinabwera kuno kudzaona wotopa ndi mphasa, sindinabwerere maliro. Wotopa: Mayi amene wangotsala pang’ono kubereka mwana. Chitsanzo: (1) Mayi wotopa amakhala wovuta. (2) Akazi awo ndi wotopa. 386