Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 384

Paphata pa Chichewa analoleranji mwamuna wakuda chonchija. Nkhani yake ndi yakuti mwamuna uja ndi wokongola m’nthumba. Wokulupala: Wojintcha, wonenepa. Chitsanzo: Mwanayu wayamba kukulupala. Wolema: Ali pafupi kubala mwana. Chitsanzo: Mayi anabwerayo ndi wolema. Wolimba m’maso: Amene sagona nsanga. Chitsanzo: Mwana uyu ndi wolimba m’maso. Wolimba moyo: Wopirira, wakhama. Chitsanzo: Mayiyu ndi wolimba moyo. Wolozeka: (a) Wokongola, wosachititsa manyazi. Chitsanzo: (1) Ali ndi ana olozeka. (2) Ukapeza mkazi wolozeka anthu amakupatsa ulemu. (b) Kulemera kapena kukhala ndi chuma. Chitsanzo: Banja lawo ndi lolozeka. Wombetsa mitu: Kudanitsa anthu. Chitsanzo: Ndani amene wawaombanitsa mitu? Wombetsa nsalu: Kulukitsa nsalu. Chitsanzo: Ndikufuna ndikawombetse nsalu yokhala ndi nkhope yanga. Womva zake zokha: Wosasamala malangizo kapena maganizo a ena. Chitsanzo: Mwamuna wako akakhala womva zake zokha pa nkhani zandalama, umafunika kumangosolola ndalama ya ndiwo kuti upangeko chitukuko. Wonekera ng’amba: Kuyaluka, kuonekera poyera. Chitsanzo: Lero ndiye waonekera ng’amba, anamugwira akupopa mafuta m’galimoto yamwini. Wonekera nyangalazi: Kuululika. Chitsanzo: Mkulu uja waonekera nyangalazi atagwidwa ali ndi mkazi wa mwini. 383