Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 38

Paphata pa Chichewa kwa mwana? Tikuthandizeni kapena kuti mkazi wanuyu akhale ndi chinja. Chinunkhira: Kusafuna zinthu chifukwa choti zakukwa- na. Ngati munthu ali ndi chinunkhira ndi zinazake ama- khala kuti akuzifuna. Chitsanzo: (1) Chakudyachi ndilibe nacho chinunkhira. (2) Maungu ndili nawo chinunkhira. Chinyanja: Amatanthauza zoyankhula, zonena kapena mawu. Chitsanzo: Atamugwira, anasoweratu chinyanja choti anene. Chinyezi: (a) Mwayi. Chitsanzo: Pakhomo pamene paja pakuoneka kuti pali chinyezi. (b) Zambiri. Chitsanzo: Anthu oyenda pansi anali chinyezi. Chinyomphiro: Mawu omwe kwenikweni amatanthauza chakumbuyo cha nkhuku, thako la nkhuku. Koma amagwiritsidwa ntchito mwachining’a potanthauza mbuyo ya munthu, thako. Chitsanzo: Koma mtsikana uja ali ndi chinyomphiro! Chionamaso: Ndalama imene munthu amalandira akaona chinachake kapena akatola chinthu. Chitsanzo: Amene atatole laisesiyo alandira chionamaso. Chionamaso: Ndalama imene munthu amapatsidwa akapeza chinthu chimene chimafunidwa. Chitsanzo: Amene atole chikwamacho n’kukachipereka 37