Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 377
Paphata pa Chichewa
Wanjatidwa: Wamangidwa.
Chitsanzo: Wakuba uja wanjatidwa.
Wankhalwe: Wankhanza.
Chitsanzo: Mkaziyu ndi wankhalwe.
Wansangala: Munthu wosangalala, Mawu akuti
mwansangala angatanthauze kulandira munthu bwino.
Chitsanzo: Akazi awo ndi ansangalala. (2) Anawalandira
mwansangala.
Wanyape: Wosafuna kukambirana koma
kumangomenyana basi kuti zithepo.
Chitsanzo: Mnyamata wachibwibwi uja ndi wanyape,
ukamamuuza zachibwana amangoyamba
kukuphaphalitsa nawo makofi.
Wanyimbo: Munthu wokondedwa kwambiri, mnzako
wapamtima.
Chitsanzo: Anakumana ndi mnzake wanyimbo.
Wapakamwa pakuthwa: Wochenjera pakamwa,
wamabodza.
Chitsanzo: Chenjera nayeni, ali ndi pakamwa pakuthwa.
Wapakamwa: Wolongolola kwambiri.
Chitsanzo: Mkazi akakhala wapakamwa, mwamuna
amayamba kukonda bawo.
Wapala: Walephera.
Chitsanzo: (1) Amakonda kujomba ndiye wapala. (2)
Amene wakhoza ndi uyu, mnzakeyo wapala.
Wapamtima: Wokondedwa kwambiri.
Chitsanzo: (1) Ameneyu ndi mwana wawo wapamtima. (2)
Alibe bwenzi lapamtima.
Wapezeka: Wadwala kwambiri, wavutika.
Chitsanzo: Komatu m’bale wathuyu wapezeka!
Wapha ulusi: Wavala bwino.
Chitsanzo: Koma ndiye mwauphatu ulusi, mukupita kuti?
376