Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 374
Paphata pa Chichewa
Wafukizi: Munthu wovuta.
Chitsanzo: Mwana wafukizi sangakhale pano, ndikhoza
kumupha.
Waimba yakale: Kuchita zothaitha, kuchedwa.
Chitsanzo: Inutu mukuimba yakale. Zinthu mukufunazo
zinatha kalekale.
Wakucha:
(a) Wochenjera.
Chitsanzo: Ana ambiri akumacha mofulumira masiku
ano.
(b) Wamkulu woti akhoza kukwatira kapena kukwatiwa.
Chitsanzo: Pakhomo pawo pali atsikana angapo akucha.
Wakula watha: Mawuwa angatanthauze kuti ndi munthu
wamkulu aziona.
Chitsanzo: Musiyeni ndi wamkulu ameneyu, wakula
watha!
Wakunjira: Munthu wobwera.
Chitsanzo: Akunjira, takulandirani! Koma musanakhale
pansi, tiyeni tikakulozereni pamene panagona m’bale
wathu.
Walemba m’madzi: Walephera.
Chitsanzo: Ngati umaganiza kuti undipusitsa, walemba
m’madzi!
Walisha n’ngwakhungu: Wosazindikira.
Chitsanzo: Koma iye uja sadziwa kuti zinthu zimenezi
n’zodula? Musiyeni, walisha n’ngwakhungu.
Walobodolobodo: Wofooka.
Chitsanzo: Ulimi sumafuna munthu walobodolobodo.
Wam’kamwa moola: Wotukwana.
Chitsanzo: Atsikana ambiri amakhala am’kamwa moola.
Wam’kamwa: Wolongolola.
Chitsanzo: (1) Azimayi onse a pamudzi paja ndi am’kam-
wa.
373