Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 37
Paphata pa Chichewa
(b) Osadziwa kanthu.
Chitsanzo: Si bwino kumapita ku mlandu chimutumutu.
Chimwanamayi: Ndi mwambo umene anthu a zikhalidwe
zina amagwirizana kuti asinthane akazi awo. Zimakonda
kuchitika pakati pa mabwenzi apamtima ndipo zimene
amachitazi zimakhala ngati abwerekana akazi.
Chitsanzo: Malinga ndi muliri wavutawu, ndi chibwana
kumachitabe chimwanamayi.
Chimwitsa: Kupereka mimba.
Chitsanzo: Mnyamatayu ndi amene wachimwitsa mwana
wa Abengo.
Chinameta nkhanga mpala: Zoopsa.
Chitsanzo: Ananena kuti akuonetsani chinameta nkhanga
mpala.
Chinasala: Chisilamu.
Chitsanzo: Sadya nkhumba chifukwa ndi a chinasala.
Chindapusa: Zimene munthu amalipira akapalamula.
Chitsanzo: Amfumu akanena kuti ulipire chindapusa cha
nkhuku ziwiri, inayo amatenga n’kukamwera mowa.
Ching’onga: Munthu wamantha. Nthawi zambiri, mawu
amenewa amagwiritsidwa ntchito ndi munthu amene
wakwiya ndipo akunena mnzake kuti ndi wamantha.
Chitsanzo: Iwe ndiwe ching’onga ndithu, khwangwala
wachabechabe.
Chinja: Mawuwa amatanthauza pakati, pathupi ndipo
ena amati mimba. Mawu amenewa amanenedwa mkazi
akatenga pakati.
Mwachitsanzo: Kodi zaka zizingodutsabe tisanamve kulira
36