Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 368
Paphata pa Chichewa
Unyopo (unyopi): Ulesi.
Chitsanzo: Unyopo umachititsa kuti pakhomo padutse
galu wakuda.
Uone kolowera: Uone kopita.
Chitsanzo: Ngati susesa m’nyumbamu uone kolowera, sin-
difuna ana aulesi pakhomo pano!
Uphungu: Malangizo.
Chitsanzo: M’pofunika kuti mwana wanuyu mumupatse
uphungu.
Upo: Msonkhano wokumana kuti muthandizane nzeru.
Chitsanzo: Ayambapo kupanga upo.
Usade nkhawa: Usavutike maganizo, usataye mtima.
Chitsanzo: Usade nkhawa, ndikuthandiza.
Usamangokhala nsidze zili tsende: Uziyendayendako.
Chitsanzo: Osamangokhala nsidze zili tsede,
kumawongolako miyendo.
Usatitsegule m’mimba! Usativutitse, usatinyanse.
Chitsanzo: Nanunso mukufuna mutitsegule m’mimba ndi
kamkonono ka wailesi mwagulayo.
Usodzi wolula: Usodzi woti ukapita kosodza subwerako
chimanjamanja.
Chitsanzo: Anzathu amachita usodzi wolula.
Utakafumbi: Mbewa.
Chitsanzo: Lero tidyera utakafumbi.
Utchisi: Uve.
Chitsanzo: Anthu a pakhomo pano ndi a utchisi.
Utsa mapiri pachigwa: Kuchititsa kuti anthu adane
kapena ayambane.
Chitsanzo: Osamachita zinthu zoutsa mapiri pachigwa.
Utsi:
(a) Munthu wopusa.
Chitsanzo: Ntchito ngati imeneyi sifuna munthu wa utsi.
367