Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 366
Paphata pa Chichewa
Ululu: Kuwawa, kupweteka.
Chitsanzo: Ndikumva ululu woopsa.
Uma manja: Woumira.
Chitsanzo: Mukapanda kuphunzitsa anawa kukhala
owolowa manja, adzakhala ouma manja.
Uma mutu: Kupanda nzeru, kusamva.
Chitsanzo: (1) Sakhoza m’kalasi chifukwa ndi wouma mu-
tu. (2) Ana anu onse ndi ouma mitu.
Uma pakamwa: Chita mantha kuulula.
Chitsanzo: Ndimafuna ndikuuzeni zinazake koma
ndangouma pakamwa.
Uma:
(a) Leka kubereka.
Chitsanzo: Akazi awo aja ndi wouma.
(b) Kutha
Chitsanzo: (1) Ntchito yawo yauma. (2) Katungeni madzi
kumjigo chifukwa mtsuko wauma.
Umandiyesa kape? Undiyesa chitsiru?
Chitsanzo: N’chifukwa chiyani ukundiyang’ana choncho?
Umandiyesa kape eti?
Umbanda: Kuba, chifwamba.
Chitsanzo: Boma lalonjeza kuti lithetsa umbanda.
Umbombo: Kumana.
Chitsanzo: Mwanayu ndi waumbombo.
Umbudza: Menya modetsa nkhawa.
Chitsanzo: Galu wakubayu ndi wofunika kumuumbudza.
Umphawi: Usiwa, kusowa, kusauka.
Chitsanzo: Ali pa umphawi wadzaoneni.
Undisamale! Chenjera nane.
Chitsanzo: Undisamale, ndikhoza kukumenya!
Undwa: Kungodikira pachabe, kupusitsidwa.
Chitsanzo: (1) Zikanakhala zayenda simukanandipeza
365