Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 364

Paphata pa Chichewa Ubwana: (a) Kukhala mwana. Chitsanzo: Ankabwera kuno ali pa ubwana wake. (b) Kukhala bwana. Chitsanzo: Masiku ano anayamba kudziona ubwana, moti kuno sabwera. Ubwenzi wonyambitana: Chikondi champhamvu kwam- biri. Chitsanzo: Anyamatawa ali pa ubwenzi wonyambitana. Uchitsiru: Kupusa, kupanda nzeru. Chitsanzo: Chitsiru ngakhale mutachisinja mumtondo, uchitsiru wakeyo sungamuchoke. Ufupiufupi: Zovala zimene atsikana komanso anyamata amakono akumavala zomwe zikumakhala zifupizifupi kapena zothina kwambiri. Chitsanzo: Ndimachita manyazi ndikamayankhula ndi mtsikana atavala ufupiufupi. Ugogodi: Kuneneza wina miseche. Chitsanzo: Mukapitiriza kuchita ugogodi akuthamangi- tsani mā€™mudzi muno. Uhule: Kugonana ndi anthu ena kuti akupatse ndalama. Limeneli ndi dzina la sipanala ina ya njinga, yomwe ima- khala ndi mabowo ambirimbiri. Sipanalayi ukhoza kukon- zera njinga yamtundu ulionse. Chitsanzo: Mtsikana akayamba kuyenda usiku, amakhala kuti wayamba uhule. Ukachenjede: Luso lapadera kwambiri. Munthu amene ali ndi luso limeneli amamutchula kuti kachenjede. Chitsanzo: (1) Ndikufuna kukachita maphunziro a ukachenjede. (2) Ndinakumana ndi kachenjede wama- samu. 363