Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 361

Paphata pa Chichewa Tsitsa mfundo: Kunena zinthu zanzeru. Chitsanzo: Mwanayu amatsitsa mfundo. Tsitsi bi!: Ali khale. Chitsanzo: “Kodi mnyamata anasiya ntchito uja akutani?” “Ali tsitsi bi kunyumbaku.” Tsitsimuka: Kumva bwino, kusangalala. Chitsanzo: (1) Mawu a Mulungu amanditsitsimula. (2) Ndipite kunyanja ndikatsitsimuke n’kukamiza nkhawa zanga. Tsitsitiza: Maliziratu zonse. Chitsanzo: Matendawo anatsitsitiza anthu onse. Tsogola: Mwalira. Chitsanzo: Achimwene aakulu aja ndi amene anatsogola. Tsokaliyenda: Munthu amene amangokumana ndi mavuto. Chitsanzo: Kodi mwakumana ndi tsokaliyenda. Tsopa mowa: Kumwa mowa wambiri. Chitsanzo: Bambo ake amautsopa mowa. Tsuka m’kamwa: Kudya chakudya chankhuli. Chitsanzo: (1) Tisungire ndalama kuti tidzatsuke m’kam- wa pa nyuwere. (2) Tiphe kalulu kuti titsukeko m’kamwa. Tsuka maso (m’maso): (a) Onera filimu, masewera enaake kapena kuona chinachake chosangalatsa. Chitsanzo: (1) Lero kuli mpira wa Buletsi ndi Manoma, ndipita kuti ndikatsuke m’maso. (2) Tiloweko m’tauni tikatsuke maso. (b) Kusukusula. Chitsanzo: Apatseni madzi kuti atsuke m’maso. Tsukuluza: Lalatira, tukwana, nyoza munthu. Chitsanzo: Si bwino kumayambana ndi munthu amene uja chifukwa akhoza kukutsukuluzani. 360