Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 36

Paphata pa Chichewa Chitsanzo: (1) Zoona mungabwere kuno chimanjamanja. (2) Osamapita kwa amfumu chimanjamanja. Chimasomaso: Uhule kapena kuchita chiwerewere. Chitsanzo: Azimayi ambiri a m’mudzi uwu ndi achimasomaso. Chimbalangondo: Munthu woipa mtima, wovuta. Chitsanzo: Pamene ankabwera kuchokera kundende anali atasanduka chimbalangondo. Chimbayambaya: Munthu wosalongosoka, munthu wopanda khalidwe. Chitsanzo: Mkazi akufuna kumanga naye banja uja ndi chimbayambaya. Chimkukuluzi: Njala ya dziko lonse. Timagwiritsa ntchito mawu amenewa tikamanena za njala yomwe sinasiye khomo. Chitsanzo: Kuvuta kwa mvulayi ndi chizindikiro choti chaka chino kukhala chimkukuluzi. Chimphona: Munthu wamphamvu kwambiri. Nthawi zambiri amakhalanso wandewu. Chitsanzo: Ndani angalimbane ndi chimphona ngati chimene chija! Chimunthu: (a) Anthu ambiri. Chitsanzo: Kumsonkhanoko kunali chimunthu. (2) Mpeni wosathwa kapena wobuntha. Chitsanzo: Mpeni wapakhomo pano ndi chimunthu. Chimutumutu: (a) Kuyenda osasenza kanthu. Chitsanzo: Mayiyo anati: “Ifetu tangobwera chimutumutu.” 35