Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 359

Paphata pa Chichewa Tsembwe (tsemwe): Kuchita mantha kapena manyazi. Nthawi zina munthu ukamachita mantha pakhungu pamatuluka timadontho tinatake, timeneto ndiye tsembwe (tsemwe). Chitsanzo: Nditangoona kuti amubaya, thupi langa lonse linachita tsembwe. Tsengera: Sintha mawu. Chitsanzo: Atamupanikiza, anayamba kutsengera. Tsetsera: Mwalira. Chitsanzo: Sindimadandaula munthu woipa akatsetsera. Tsika: (a) Vina mwaluso. Chitsanzo: Mtsikana uja akati atsike, simungamukonde. (b) Munthu amene amadwala akatsirizika. Chitsanzo: Munthu timanena kuti wadwala kwa nthawi yaitali uja akuti watsika tsopano. Tsilira mang’ombe: Kuwonjezera zina kuti nkhani ikome, kupokolezana nyimbo. Chitsanzo: (1) Ndati nditsirirepo mang’ombe za munthu mwatamulayo. (2) Pamene ena amaimba, ena amatsirira mang’ombe. Tsilira mavume: Kuwonjezera zina kuti nkhani ikome, kupokolezana nyimbo. Chitsanzo: (1) Ndati nditsirirepo mavume za munthu mwa- tamulayo. (2) Pamene ena amaimba, ena amatsirira mavume. Tsina khutu: Kuululira munthu zinazake. Chitsanzo: (1) Bwerani pang’ono ndikutsineni khutu za munthu akubwerayo. (2) Mwamva zimene zachitika kumtundaku? Tabwerani kuno ndikutsineni khutu! 358