Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 358

Paphata pa Chichewa Tsakamuka: (a) Kugwa modetsa nkhawa. Chitsanzo: Anatsakamuka mumtengo wamango. (b) Kuchoka paudindo. Chitsanzo: Anatsakamuka paudindo wawo. Tsala madzi amodzi: Kutsala pang’ono kufa kapena kutha. Chitsanzo: (1) Ndinadwala kwambiri moti ndinangotsala madzi amodzi. (2) Nyembazi zangotsala madzi amodzi. Tsala: (a) Malo osalimidwa. Chitsanzo: Anapha njoka pa tsala lija. (b) Kuuza munthu kuti asakutsatire. Chitsanzo: Tsala, kunjaku kwada. Tsamira mkono (gonera dzanja): Mwalira. Chitsanzo: (1) N’zachisoni kuti bambo aja atsamira mkono. (2) Mudzandilira ndikadzagonera dzanja. Tsanura: Kupungula. Chitsanzo: Titsanunireni mafutawo. Tsatanetsatane: Molongosoka, motsatira dongosolo lake. Chitsanzo: Tafotokozani mwatsatanetsatane. Tsekera mbewa kuuna: Tsekereza zokoma. Chitsanzo: Anthu amafuna kukuthandizani inu n’kuwaberanso! Mwatsekereza mbewa kuunatu pame- nepa! Tsekera: (a) Pumira kaye, maliza kuti udzayambenso nthawi ina. Chitsanzo: Ana atsekera sukulu. (b) Udzu wokhwima bwino. Chitsanzo: Akukadula tsekera. Tseketseke: Kumva bwino, kukoma, kuzuna, kutsekemera. Chitsanzo: Mzimbeyi ili tseketseke. 357