Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 356

Paphata pa Chichewa Tibula: Kumenyedwa kwambiri. Chitsanzo: Akachita masewera ndimutibula. Tichedwepo: Tikambirane bwinobwino, tionetsetsepo bwinobwino. Chitsanzo: Koma pa nkhani iyi yokha tichedwepo. Tigwira mtengo wanji? Mawuwa amanenedwa munthu akamadandaula kuti achita bwanji, kapena akathedwa nzeru n’kumasowa chochita. Chitsanzo: Njala imeneyi kaya tigwira mtengo wanji! Tigwire mtengo wanji? Titani, tichite chiyani? Chitsanzo: Ndalema nazo, kaya ndigwire mtengo wanji? Timere mizu: Kukhazikika. Chitsanzo: Mkamwini ameneyu wamerapo mizu pakhomo pano. Titere: Mawuwa amayankhulidwa munthu akamapereka chinachake, chinthu kapena moni. Chitsanzo: Panja ndinabwereka ndalama zanu eti? Ndiye titeretu! (2) Tiwapatse kaye moni athuwa! Titeretu! Titimira: Lowa m’matope, kanirira. Chitsanzo: Galimotoyo imangovinavina m’matope, kenako inatitimira. Tiuzeni pamene mwaima! Tiuzeni maganizo anu. Chitsanzo: Popeza mwamva nkhawa yathu, tiuzeni pame- ne mwaima. Tiyi wopanda zida: Tiyi wopanda chomwera. Chitsanzo: Akungomwa tiyi wopanda zida. Tola m’kamwa: Kufufuza zolakwa m’zokamba za anthu. Chitsanzo: Amabwera kuno kuti adzangonditola m’kam- wa. Tola nkhwangwa ndi mpini womwe: Chita mwayi waukulu kwambiri. Chitsanzo: Anzathu mwatola nkhwangwa ndi mpini wom- we, kodi munasamba pati? 355