Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 354
Paphata pa Chichewa
Thudzula gule: Kumenya munthu kapena kuchita
ndewu.
Chitsanzo: Akachita masewera tithudzula gule.
Thudzula: Menya modetsa nkhawa.
Chitsanzo: Akapitiriza kundiputa ndimuthudzula.
Thukuta liri kamukamu: Ali thukuta lokhalokha.
Chitsanzo: Ndinakumana nawo ali thukuta kamukamu.
Thula: Khala chete.
Chitsanzo: Thula! Wati amanena chiyani?
Thumba lobooka: Mawuwa amanenedwa pofotokoza
munthu amene sasunga ndalama.
Chitsanzo: Mavuto andichulukira moti ndikugwira ntchito
molimbikira koma ndikungokhala ngati ndikulandirira
ndalama m’thumba lobooka.
Thumuka: Kuduka kwa ulusi kapena chingwe.
Chitsanzo: (1) Ulusiwu suchedwa kuthumuka. (2)
Tathumulani ulusi wangoti yaviyaviwo.
Thunga:
(1) Kalichero kakang’ono.
Chitsanzo: Apakulira nsima m’kathunga.
(2) Dzina la njoka.
Chitsanzo: Panadutsa thunga apa.
(c) Munthu wokonda kukhala m’nyumba. Thunga ndi
njoka imene imakonda kukhala kuuna wake osatuluka
kunja.
Chitsanzo: Nankhoma ndi thunga, amachita manyazi
kukhala pagulu la anthu.
Thunza mtima: Dekha.
Chitsanzo: Thunzani mtima achimwene, musapupulume.
Thupi (chithupi): Kunenepa.
Chitsanzo: Mayi awo ndi a thupi.
Thupi lolagala: Thupi lokhwima.
Chitsanzo: Mwanayu ali ndi thupi lolagala.
353