Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 352

Paphata pa Chichewa Thawa mfuwu wake womwe: Kudabwa zimene wanena wekha. Chitsanzo: N’chifukwa chiyani amathawa mfuwu wake womwe? Thawitsana: Kutengana kwa mwamuna ndi mkazi n’kupita kutali n’kumakakhala limodzi monga banja. Chitsanzo: Anathawitsana ndi mwamuna wa eni. Theka: (a) Kugwidwa. Chitsanzo: Mbava imatibera ija yatheka lero. (b) Kutoperatu. Chitsanzo: Anawa atheka, pitani mukawagoneke. Thendo: (a) Mtedza kapena zinthu zokometsera ndiwo kapena chakudya china. Chitsanzo: Mundiwozi atsiramo thendo. (b) Mawu kapena nkhani yongowonjezera. Chitsanzo: Munkhaniyi awonjezeramo thendo. Thephethephe: Chamadzimadzi. Chitsanzo: Waphika nsima yathephethephe. Thima: (a) Kumwalira. Chitsanzo: (1) Chigawenga chija chathima. (2) Limbikira kugwira ntchito kuti ukadzathima, tidzagawane chuma chakochi. (b) Kuledzera kwambiri. Chitsanzo: Amangodzikodzera akathima. (c) Kusiya kuganiza, amakhala ngati sakudziwa chimene chikuchitika, amasokonezeka. Chitsanzo: Bambowa nthawi zina amathima. Thimbwidzika: Kuyenda monyada, kuvina kwambiri. Chitsanzo: (1) Ndinakumana nawo akuyenda moth- imbwidzika. (2) Ndinawapeza akuthimbwidzika. 351