Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 346

Paphata pa Chichewa Takasa: Kusokoneza zinthu. Chitsanzo: Bwana woyamba anangotakasa zinthu n’ku- chokapo. Takata: (a) Gulitsa kwambiri. Chitsanzo: Koma ndiye mwatakatatu lero! (b) Kukhala ndi khalidwe lachimasomaso. Chitsanzo: Watakata amuna ambiri mkazi ameneyu. Takataka: Gwira ntchito, phika chakudya. Chitsanzo: (1) Mkazi amafunika azitakataka. (2) Musachoke, mayi akutakataka kuseriku. Takuonanitakuonani! Mawu aulemu omwe anthu amanena akamadutsa munthu. Mawuwa ayamba kulowa m’malo mwa “wawa.” Chitsanzo: Takuonanitakuonani! Kaya muli bwanji? Talikira: (a) Suntha pano. Chitsanzo: Talikira, ndingakukankhe. (b) Kuchokapo kupita kwina. Chitsanzo: Amenewo simunawapeze, atalikira! Tama ine: Yamika ine. Chitsanzo: Uzitama ine, zikanakuvuta ndikanapanda kukhalapo. Tama mano: Tama nzeru, chuma, mphamvu ndi zina osati za wina. Chitsanzo: Ukamafuna kuchita chinachake, umatama mano. Tamba: Mawu amenewa amagwiritsidwa ntchito aka- manena zokhudza zikhulupiriro za ku Africa kuno zo- khudza ufiti. Chitsanzo: (1) Mfiti zojaira zimatamba masanasana. (2) Akungokhala ngati awagwira akutamba. 345