Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 344

Paphata pa Chichewa Sumbudzula: Kumenya, kukhaulitsa. Chitsanzo: Ukabweranso usiku ndikusumbudzula. Sunga khosi: Pirira zokoma zikubwera. Chitsanzo: Ngati ukufuna udzakhale ndi tsogolo labwino, sunga khosi. Nanga ungadzavale mkanda woyera khosi ulibe? Sunga mwana: Sunga zinthu zofunika kwambiri, thawitsa zako. Mawuwa amanenedwa choopsa chikamabwera. Chitsanzo: Zikakuvuta ukhoza kugulitsa zonse, koma osaiwala kusunga mwana. Sungakhumbire: Sungasirire, sungazifune. Chitsanzo: Sungamukhumbire utaona zimene amachita. Sungulumwa: Kusowa wocheza naye. Chitsanzo: Mukachokapo ndimasungulumwa. Sunsunuka: Kukula. Chitsanzo: Tsopano mwasunsunuka, mukufuna mutisowetse mtendere. Sunyenyeka: Suvutika kapena kumva kupweteka. Chitsanzo: Ngakhale chibwenzi chitatha, sind- inganyenyekeyi. Sunzumira anthu: Kukaona anthu kwa nthawi yochepa. Chitsanzo: Ndakhalitsa m’tauni muno, mpofunika ndipi- teko kumudzi ndikawasunzumire anthu. Supula: Kuputa mkwiyo kwambiri. Chitsanzo: Andisupula, adziwanso kuti ndine Nasimango. Suwa: Kuchoka kapena kuperepeseka kwa khungu. Chitsanzo: Khungu lawo likusuwa. Swera mphanje: Kuwonjezera mabodza. Chitsanzo: Usamachite kufotokoza moswera mphanje. Swetsa mutu (iswa mutu): Chopatsa maganizo kwambiri, kuganiza mozama. Chitsanzo: Nkhani imeneyi ikundiswetsa mutu. 343