Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 343

Paphata pa Chichewa Sowa yamchere (yasopo): Kusowa ndalama, kuvutika. Chitsanzo: Azibusa ambiri akudya bwino, koma nkhosa zawo zikusowa ndi yamchere yomwe. Sowa zochita: (a) Kumangoyendayenda, kumangochita zinthu zosafunika kwenikweni. Chitsanzo: Chifukwa cha kusowa zochita anthu ambiri amavala gule. (b) Kukhala popanda ntchito yoti ugwire. Chitsanzo: Dzulo ndimasowa chochita. Sudziwa mtima wamoto: Sudziwa zomwe zitachitike, mwina chipserera. Chitsanzo: Papsa tonola sudziwa mtima wamoto. Sudzula: Kuuzidwa kuti udzipita kwanu banja litatha. Chitsanzo: Powasudzula anawapatsa 3 kwacha n’kuwau- za kuti adzipita kwawo. Sukulu yamkaka: Sukulu ya ana aang’ono kwambiri. Anazipatsa dzinali chifukwa anawo amamwa mkaka. Chitsanzo: Boma latsegula sukulu zamkaka. Sukulu yankombaphala: Sukulu ya ana aang’ono. Chitsanzo: Chaka chamawa akayamba sukulu yankombaphala. Sula mwana: Kuphunzitsa mwana makhalidwe abwino. Chitsanzo: Ana anuwa munawasula bwino. Suluka: (a) Kuchoka mtundu. Chitsanzo: Nsaluyi ndi yosuluka. (b) Kutha mphamvu. Chitsanzo: Mankhwalawa anasuluka. Sumbudzuka: Ng’ambika, sosoka, fwifwa. Angatan- thauzenso kubwera usakuoneka bwino. Chitsanzo: (1) Andipatsa malaya osumbudzuka. (2) Abwera atasumbudzuka. 342