Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 342
Paphata pa Chichewa
Solola ndalama: Kuba ndalama zochepa.
Chitsanzo: Ena akamapakula ndalama, ena amangosolola
pang’ono.
Sololoka mlomo: Munthu wa mlomo waukulu.
Chitsanzo: Amakonda kutsonya, n’chifukwa chake ali
wosololoka mlomo.
Songo: Munthu wabwino pamaso, koma kuseri
amakukonzera chiwembu kuti akuphe kapena
kukunenera mabodza.
Chitsanzo: Chenjerani, munthu ameneyu ndi songo.
Sosolera pamsampha: Chenjeretsa.
Chitsanzo: (1) Sindifuna kuchita zinthu ndi ameneyu,
amakonda kusosorera pamsampha. (2) Mnyamata
ameneyu amakonda kusosolera pamsampha.
Sosora nthenga: Mawuwa amanenedwa ndi munthu
amene anali ndi udindo kapena mphamvu zinazake ndiye
mphamvuzo zinatha kapena ena anamuchotsera
mphamvuzo.
Chitsanzo: Ife anatisosora nthenga, sitilinso ndi mphamvu
ngati kale.
Sowa chochita: Sowa chonena, kungokhala osachita
kanthu.
Chitsanzo: Atamupanikiza ndi mafunso, anangoti
nyotcholo, kusowa chochita.
Sowa cholaza: Kutsatira khalidwe lolakwa la kumaloko.
Chitsanzo: Ukapita pa mudzi wa zidakwa, umasowa chola-
za.
Sowa pogwira: Kusowa chochita pamavuto.
Chitsanzo: Matenda akalowa pakhomo umasowa pogwira.
Sowa tulo: Kukuvutika maganizo koopsa, kuchititsa kuti
usagone.
Chitsanzo: Nkhaniyi imamusowetsa tulo.
341