Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 34
Paphata pa Chichewa
wamwini ndiye anthu apita kukakambirana za nkhaniyo
kwa munthuyo. Anthuwo akafika, eni pakhomopo
amanena kuti awalipire chikhalamumthunzi kuti
amasuke kunena chomwe abwerera. Akapereka malipiro
amenewa mpamene mlanduwo umayamba.
Chitsanzo: Musananene zambiri, yambani kaye
mwatipatsa chikhalamumthunzi.
Chikhwaya: Munthu wolemera.
Chitsanzo: Malo ano kumabwera zikhwaya zokhazokha.
Chikondi cha bulangete: Chikondi chachikulu kwambiri.
Chitsanzo: Chikondi cha amene aja ndi cha bulangete.
Chikondi chobwerekana nsalu: Kugwirizana kwambiri.
Chitsanzo: Chikondi chawo ndi chobwerekana nsalu.
Chikulowa kudzino: Chikukopa moti uyamba
kuchikonda kwambiri.
Chitsanzo: Ukadzangodya bokho kamodzi, adzakulowa
kudzino.
Chikumbumtima:
(a) Munthu wamkati amene amakuletsa ukamafuna
kuchita zoipa komanso amakuimba mlandu ukalakwitsa.
Chitsanzo: Atapha munthu, chikumbumtima chake
chinayamba kumuvutitsa.
(b) Kukumbukira zinthu.
Chitsanzo: Mayi uja ali ndi chikumbumtima, ukamuuza
zinthu saiwala.
Chikwanekwane: Kusasowa kanthu.
Chitsanzo: Ukamapita kutali umafunika kumayenda
chikwanekwene.
33