Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 339
Paphata pa Chichewa
(b) Kupha zonse kapena kuchotsa zonse.
Chitsanzo: (a) Chitopa chasesa nkhuku zonse. (b) Matend-
awa akhoza kusesa mudzi wonse.
(c) Kuchotsa zinyalala ndi tsache.
Chitsanzo: Sesani pabwalo padutse chintali.
Sewera ndi pakamwa: Yankhula zinthu zoti ukhoza
kupalamula nazo.
Chitsanzo: Munthu ameneyutu akusewera ndi pakamwa,
zoona kumanyoza mtsogoleri wadziko?
Sewera paulimbo: Kuchitsa zinthu zomwe ukhoza
kupalamula nazo, kuputa munthu.
Chitsanzo: (1) Bambowa akusewera paulimbo, akachita
masewera amangidwa. (2) Iwetu ukusewera paulimbo,
akhoza kukuonetsa chinameta nkhanga mpala.
Shasha (syasya):
(a) Munthu wolemera.
Chitsanzo: Usayese kupikisana mavalidwe ndi amene uja
chifukwa ndi shasha.
(b) Munthu wochangamuka kapena wochenjera.
Chitsanzo: Awa ndi mashasha a m’tauni muno.
Shomola nkhandwe: Palamula.
Chitsanzo: Anyamata amene aja amupha, washomola
nkhandwe.
Shosholo: Kuyendera limodzi.
Chitsanzo: Amayenda shosholo ndi akazi awo.
Shupa: Kuvutitsa.
Chitsanzo: Munthu ameneyu amandishupa kwabasi.
Si masewera: Ndi patali, ali ndi luso kapena amachita
bwino zinazake.
Chitsanzo: Mwamuna wawo uja si masewera.
Si zocheza: Ndi patali.
Chitsanzo: Nsapatoyi si zocheza.
338