Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 338

Paphata pa Chichewa Sauka: (a) Kumwalira kwa wina wa m’banja. Chitsanzo: Pakhomo pano tinasauka chipitireni achimwene athu aja. (b) Kutha kwa chuma, kukhala opanda ndalama. Chitsanzo: Ambiri omwe anali olemera asauka. (c) Kuvutika. Chitsanzo: Akusaukabe ndi matenda aja. Sawa: (a) Kuwawa. Chitsanzo: Simunabwere kudzationa moyo utasawa. (b) Kufika povuta kwambiri. Chitsanzo: Kuntchitoku kwasawa. (c) Kukhala choti sichingapse, kukhala chamadzi ambiri. Chitsanzo: Chinangwachi ndi chosawa. Sekerera ku khudu: Sekerera utayang’ana kumbali. Chitsanzo: Mukundinena eti? Nanga n’chifukwa chiyani mukusekera ku khudu. Sekereren’kudyeremwana: Munthu wachinyengo. Chitsanzo: Amene uja ndi sekereren’kudyeremwana. Seleula: Kunena munthu monyoza. Chitsanzo: Ndinawapeza akuseleulana ndi alamu awo. Senda: Menya kwambiri. Chitsanzo: Akusendatu! Sendera: Yandikira. Chitsanzo: Sendera pafupi ndikunong’oneze. Senza: Mwalira. Chitsanzo: Amfumuwo azunzika kwa kanthawi, lero asenza. Sesa: (a) Kufala, kukhudza ambiri. Chitsanzo: Njala imene ija inasesa mudzi wonse. 337