Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 337

Paphata pa Chichewa Sandiona bwino: (a) Amaoneka kuti amadana nane. Chitsanzo: Munthu ameneyu sandiona bwino. (b) Amandikayikira. Chitsanzo: Munthuyu sindimuona bwino. Sanduka luzi: Kuonda kwambiri. Chitsanzo: Msungwana ankapukusika uja simungamudziwe lero, anasanduka luzi atatenga ka- chilombo. Sanduliza: Tembenuza, kusintha munthu. Chitsanzo: Akufuna kukusandulizani. Sangandithe: Sangandisinthe, sangalimbane ndi ine. Chitsanzo: Ngakhale alimbane nane, sangandithe. Saona ndi maso: Munthu wakuba. Chitsanzo: Anthu ena saona chinthu ndi maso. Saonandege: Nkhumba. Chitsanzo: Akufuna ndikawakonzere saonandege. Sapita m’thumba: Satulutsa ndalama. Chitsanzo: Anthu ena akapita kumowa sapita m’thumba, amangodikira kuti anzawo aziwagulira. Sasatuka: Kuyerekedwa, kudzikweza, kudzimva. Chitsanzo: Si kale pamene anayamba kusasatuka. Sasira nkhani: Kunamizira munthu wina wosalakwa. Chitsanzo: Munthuyu ndi wosalakwa, nkhaniyi angomu- sasira. Sasunga pakamwa: Munthu wosabisa kanthu kapena wosasunga chinsinsi. Chitsanzo: Amene ajatu satha kusunga pakamwa. Satha phazi: Amabwera kawirikawiri. Chitsanzo: (1) Waona chiyani kuti asamathe phazi pakhomo pano. (2) Achimwene anu satha phazi pakhomo pano. 336