Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 331
Paphata pa Chichewa
Ponya nkhwanga n’chambuyo: Ndi osabereka kapena
kuti chumba.
Chitsanzo: Amene aja anaponya nkhwangwa n’chambuyo,
n’chifukwa chake m’nyumba mwawo mulibe wailesi.
Ponya patsogolo: Thandiza.
Chitsanzo: Ndimasowa mtengo wogwira moti
mwandiponyera patsogolo.
Ponya sitepe: Vina.
Chitsanzo: Ndinadabwa nditamuona akuponya sitepe pa
ukwati.
Potola: Kupha.
Chitsanzo: Amene wandibera miyono yanga wandipotola.
Potoza: Kusemphanitsa zinthu, kuvala nsapato mwendo
womwe si wake, kuchita zinthu mosayenera.
Chitsanzo: (1) Mwanayu wapotoza nsapato. (2) Anthuwa
amapotoza mawu a Mulungu kuti zigwirizane ndi mfundo
zawo.
Psanga: Kuba, kutenga zambiri kuposa ena.
Chitsanzo: (1) Zonse zomwe ali nazozi n’zopsanga. (2)
M’malo moti tigawane mwachilungamo akumangopsanga.
Psereza nalo bodza: Namiza kwambiri.
Chitsanzo: Iye amangomvetserabe, samadziwa kuti
akumupsereza nalo bodza.
Psete:
(a) Kuyankhula mosaopa, mosabisa mawu.
Chitsanzo: (1) Amayankhula mopanda psete. (2) Bamboyu
alibe psete.
Ponda pamutu:
(a) Kubadwa pambuyo pa woyamba.
Chitsanzo: Mwana uyu anaponda pamutu pa uyu.
(b) Nyoza.
Chitsanzo: Ife ndiye amangotiponda pamutu.
330