Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 326
Paphata pa Chichewa
(b) Kulimbana, kusamvana.
Chitsanzo: Pakati pawo pali phote.
Phovomora: Kumenya modetsa nkhawa.
Chitsanzo: Mkazi wa m’kamwa uja anamuphovomora dzu-
lo.
Phukusi: Chinthu chokulungidwa munsalu kapena
chinachake.
Chitsanzo: Nyamulani kaphukusi kanuka.
Phula ngozi: Menya munthu, vulaza munthu, chita ngozi.
Chitsanzo: Mutengeni mwana wanuyu akhoza kundiphu-
litsa ngozi.
Phula utsi: Kunena zinthu zimene sukuzimvetsa.
Chitsanzo: Mayi aja amaphula utsi.
Phula:
(a) Munthu wopusa.
Chitsanzo: Sukulu imafuna mwana wochangamuka osati
phula.
(b) Kupeza chuma.
Chitsanzo: Anzanu aja anaphula.
(c) Kuchotsa chinthu pamoto.
Chitsanzo: Aphula nyemba zosapsa.
Phuliphuli: Kukongola, kuoneka bwino.
Chitsanzo: (1) Phuliphuli si njinga koma tcheni. (2) Phu-
liphuli ameneyu mukulowera kuti?
Phulitsa: Menya modetsa nkhawa.
Chitsanzo: Wayambanso kugeya mwano, ndikhoza ku-
kuphulitsatu!
Phulusika: Kukalipa.
Chitsanzo: Ndinawapeza akuphulusika, maso ali piriwiri
ndi ukali.
Phuma: Kuchita zinthu mosaganiza bwino, wopupuluma
pochita zinthu, wolongolola.
325