Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 324

Paphata pa Chichewa Chitsanzo: Anangodziponya m’madzi kuti phava! Phava: Zinthu zambiri, la nthochi. Chitsanzo: (1) Amumenya kaphava ka makofi. (2) Eko phava la nthochi. Phazi limodzi: Mwamantha. Chitsanzo: Pakhomo paja ndimapita ndi phazi limodzi. Phazi ndiombole: Kuthawa. Chitsanzo: Ukaona kuti zavuta umafunika kungopempha kuti phazi likuombole. Phazi thandize: Kuthawa zitavuta. Chitsanzo: Zitavuta ndinangoti phazi thandize. Phazi: Kuyenda kapena kupita kwinakwake. Chitsanzo: Phazi lako lisamapitepite kwa mnzako chifu- kwa akhoza kutopa nawe n’kuyamba kunyansidwa nawe. Pheka: Kutheka, kugwidwa. Chitsanzo: Wakuba amavuta uja lero wapheka. Pheramphongo: Kutsirira ndemanga pankhani, kugwiri- zana ndi zimene wina wanena. Chitsanzo: Ndikufuna kupheramphongo zimene achikulirewo anena. Pherera: Kudziteteza, kudzitchinjiriza. Chitsanzo: Amawayankha mowapherera. Phesi. Munthu wopanda mphamvu. Chitsanzo: Ukakhala phesi ndi bwino kungokhala chete poopa kudziputira mavuto. Phethira: Kungopusa pang’ono. Chitsanzo: Mukaphethira akuyeretsani m’maso. Phika maso: Kunyada kwambiri. Chitsanzo: Atsikana a masiku ano ukawauza nkhawa za- ko, akumangophika maso kenako n’kukutsonya. 323